KUMANGA NDI MILIMO

MPINGO NDI CHIANI NDI MKRISTO?

Mpingo oona omangidwa ndi miala ya moyo umene Yesu amaiona, naikonda iyenela yopangidwa ndi zisulo zabwino.

7/5/2006

Baibulo limatiphunzitsa kuti Mulungu sakhala nyumba zomangidwa ndi manja a anthu. Aefeso 2 ndi mbali zina za Baibulo zimati ife ndife malo okhalamo Mulungu mwa mzimu—mpingo. Pamene muyenda kapena kuyendetsa pa mseu, mukhoza kuzindikila zomanga za chipembedzo chifukwa ndi zooneka motelo, koma, poti mpingo weniweni ndi omangidwa mwa anthu, osati zomanga, ndiye umaoneka motani? Mungazindikile bwanji mpingo oona ndi onama?

Mumpingo wachipangano chakale, umakhala membala chifukwa choti makolo ako ndi (Ayuda) ngati umakhulupila chinthu chabwino ndipo makolo ako ali mbali ya mpingo, ndiye, iwe “umakhala mu mpingo” nthawi zonse, ndi kupeleka chakhumi, pamenepo inu mumakhala a mu ‘mpingowo’.

Mumpingoyo chipangano chatsopano wa Yesu, zimenezi sizoona. Muyenela Kupeleka Moyo wanu kwa Mulungu. Uneneli wa mu chipangano chatsopano umati kuti mpingo umene Mulungu akumanga (Yeremiya 3, Aher 8, Heb 10) ndiwo mpingo weniweni owona, umene ang’ono mpaka akulu onse adziwa Mulungu mpingo ungadziwike mu njira imeneyi. Kuchotsela apa ndi chipembedzo chabe (chokhala chimene opumulitsidwa achita chabe) koma osati ndi mpingo oona wa Yesu Kristo choikapo nyali, ngati ali anthu achita ndi kuonelela chimene chilli kale osati kulumikizidwa kwa moyo pamodzi (1 Akolinto 12)

Mpingo oona omangidwa ndi miala ya moyo umene Yesu amaiona, naikonda iyenela yopangidwa ndi zisulo zabwino. Ngati nyumba imangidwa ndi zitsulo zosalimba, mudziwe kuti idzagwa ngati mitengo wogwilizitsila ndi yoola, idzagwa pansi. Njerwa zofewa zosaumbidwa bwino, kapena zopangidwa ndi zosalimba sizingathe kuthandiza kulemela kwa denga ndipo idzagwa. Monganso, ngati tiyesa kumanga nyumba ya Mulungu muzomangila zosalimba, idzagwanso ndithu ngati munthu sadziwa Mulungu, sangakhale otsatila mpingo wa Yesu ngati nyumba imene Mulungu akumanga kuchokera kwa Amuna ndi Amayi idzakhale yotheka kuima, siiyenela kukhala miala yoipa pa nyumbayi. (1 Akorinto 3 : 3–5).

Koyenela mpingo, kapena onse pamodzi, potero opanda chilema? Inde sizophweka ayi (1 Yohane 1) koma kolingana ndi mau a Mulungu, chofunikila ndi ichi: onse ochuluka mwa abale—“akonde kuunika” “akonde choonadi” ndipo akhale kuona mtima kwenikweni mwa Mulungu mu njira imene “thupi ndi mwazi—sizinaulilire” inde, ndizo zofunikira (Mateyu 16:16–18, Yohane 3:19–21, 1 Yohane 1–3, Eze 11:19, Yeremiya 31:34, Eze 36:26) Zimenezi ndi zimene Yesu anati adzamanga mpingo wake pamenepo, ngati uli wakedi. Zina zake zidzakhala ngati kumanga pa nyumba ndi njerwa zosalimba kapena matabwa mu dziko lapansi, ndipo Yesu adzagwilitsa mitengo woona pomangila nyumbayi.

Kenanso aka kuti sikuti munthu aliyense ali wabwino. Koma, zithandauza munthu, akonde ndi kumvera Yesu ndipo sanyosera kuthandiza kwa ena, amene afuna kuthandiza iwo kukonda ndi kumvera Yesu, afuna kuthandizika zomangila zabwino za nyumba ya Mulungu ndi pamene munthu amene safuna chithandizo iye amati, “ osandiweluza ine” “samala zako amaziteteza,” “chotsa choipa m’maso mwako” zimenezo ndi zomangila zoipa, zimene Mulungu salora mnyumba yake. Yesu sadzamanga nyumba yake motelo. Iyi ndi mitengo wowola ndipo udzadulidwa pakati pa anthu. (Machitidwe 3:23, Mat 18, 1 Akorinto 5) Mu mpingo woona amene atelo saloledwa. Ngakhale atakhala ndi ndalama zochuluka, kapena amadziwa Baibulo motani angakhalenso mtsogoleri” koma ngati sabvomeleza mpingo wa Yesu mofewa ku chiphunzitso cha Yesu, ndiye sangakhale ku mbali ya mpingo woona umene uchitika mu mzimu. Ngati akana, chikondi ndi kupepsa nzeru, kuthandiza ndi kudekha mtima, ndi kuwalola kukhala pakati pa abale ndiye tikutsutsa Yesu ngakhale malamulo ake.

Ngati wina ndi woomboledwa, ayenela kukhala ndi Mzimu woyela (Aroma 8:9, Agalatiya 3, Aefeso 1) ndipo kudziwa kuti ali ndi Mzimu Woyela mwa iwo (angakhale ndi umboni otani ndi kuti, “Ambuye” Mateyu 7) amakonda kumvela. Ali olengedwa atsopano ndikukonda kuwala ndi kukonda choonadi

(2 Atesolonika 10) ndipo monga “makanda obadwa kumene” amakhala ndi mau a Mulungu kuchitidwa mu moyo wawo (1 Petro 2) ngati munthu ali ndi Mzimu wa Mulungu amakonda kuunika ndi choonadi, ndipo makhalidwe awo amayamba kusintha. Amalapa mmene amakhalila ndi akazi awo kapena amuna awo, ndipo amasinthikadi. Amasintha mmene amakhalira ndi antchito awo, kapena ana awo, anzawo azungulila nyumba zawo, ndipo amasintha. amalapa machimo awo akale ndi makhalidwe oipa amasinthadi, ndi kukula msinkhu.

Mphatso ya mzimu oyera ndilo dipo la cholowa chawo “chinthu ndiwo cholamulidwa chawo” atero Yesu, mu Yohane 3. Ichi ndi chimene chimasiyanitsa olungama kuchionongeko. Sikuti onse ndi olungama, koma iwo amene akhululukidwa onse. “Akonda kuwala, ali ndi mphatso ya Mzimu woyera umene adalibe kale. Tsopano kuchokela pansi pa mitima ya mwala, yakhala ofewa kuchokela pansi pa mitima ya mwala, yakhala ofewa kuchokela pansi pa mtima, Mulungu wapangitsa kumvela malamulo ake. Kuchosela pansi pa mtima amasamala mau a Yesu pa makhalidwe. Nkhosa zimamva mau a Mbusa chifukwa ali ndi mzimu wa Yesu.

Nkhosa inena “ine ndifuna Yesu! Ndilondolereni ine njira imeneyo.” Mbuzi inena, “ndisiyeni ine ndekha! Ndikhoza kuchita chozizwa! Ndikhoza kupereka ndalama zanga kwa aphawi! Ndimadziwa zinthu ndekha. Ine ndili bwino kuposa inu, ndipo sindisamala zomwe munene.”

Mukhristu, ogawana nawo wa pangano latsopano, akonda chilungamo (2 Atesalonika 2:10) ndipo akonda kuwala (Yohane 3:19–21), ndipo tsopano ndi ogawana nawo chilengedwe cha Uzimu” (2 Peter 1:4, Aroma 6:1–14). Icho ndicho chizindikiro choti Mzimu ukhala mwa iwo kapena mwa aliyense waife. Ife sitiyenera kulenga mau a wina aliyense poti chifukwa anena, “Ambuye! Ambuye!” Yekha munthu amene azitaya yekha ndipo amoyo kwa Yesu ndi kuti iwo anena akhudzidwa ndi kumwamba ndipo akhala mwa mulengi wa dziko ali opulumutsidwa mowonadi ndi “membala” wa Mpingo wake (Aroma 8:9–11, Luka 9:57–62, Yohane 1:12–13, 3:16–21, 1 Yohane 3:8–10, 5:18–20).

Choikilapo nyali chenicheni mu chowonadi, mpingo weniweni uli ndi malire (“monga muzikwi zikwi wa mamembala!”) kwa iwo akhala ndivumbulutso la mwana “kuti thupi ndi mwazi sizidavumbulitsa, koma Atate yekha kumwamba wavumbulutsa kwa iwo.” Sizokhudza chifupi, kapena chidziwitso kapena kuzipereka kapena kukulitsa. Ndidzakhudzana ndi kukumana ndi Mulungu tate, mu umunthu wa Mwana wake, pamene imfaibala moyo onga wa Mulungu watunthu kuchoka popanda kanthu (Yoha 3:5–8, 12:24, Aroma 6:1–14, Agalatiya 6:14–17) ndi zoonadi alipo ena ochepa amene afuna chobvala ndi enanso amene akuganizira mwa “ chaka chonse” chawo (Yoh 13:8–9, Yoh 15, Yoh 2:19, Yuda 11–25)

Ife mwina tili ndi moyo wodabwitsa ndi iye ndiponso ndi wina ndimnzake, kapena si—Ukhristu wolembedwa m’ Baibulo ndi silili mpingo wolembedwa. Indetu alipo anthu ena opulumutsidwa amene akhala m’magulu amene siali mipingo yoonadi, ngakhale adzitcha okha mipingo. Iyo ndinkhani yinanso ife tikunene kuti sitikhudza mpando wake wachifumu (ife tingokhuzako umunthu wathu ndi kuzitenthetsa ngati ife sitikhala pamodzi m’moyo wapamwamba wa Mulungu). Nthawi ndi nthawi kulumikizidwa ku mutu ndi kwawina ndi mnzake! Mwambo umene “uchitika popatsa iye ulemu wake” kapena kuti tiphunzire mfundo za iye, kapena kuti tiyitane zofuna za thupi kuchokera kumwamba ndi nyimbo zathu—mwa ngati mbiri, izi zasintha miyoyo yochepa chabe mwa chithudzi cha Mwana. Ife mwina tikugawana mu zinthu za Umulungu pamodzi tsiku ndi tsiku, kapena simoyo wosatha ayi, kapena choyimikira nyali ndi mpingo, ngati mmene Mulungu adachipangira. “ chotupitsa chochepa chitupitsa mkate WONSE.”

Ife tisakhale ngati makanda amene amanena zinthu zoona, koma sakhala ngati Yesu. Ndipo, mpingo simsonkhano wa onga akhristu amene amanena zinthu zoona koma alibe Mzimu wa Yesu mkati mwawo, ngati munthu. Yesu ndiwomanga wamkulu. Iye sadzamanga ndimwala wofewa ndi thabwa lovunda ayi. Iye afuna kumanga nyumba ya ulemelero kukhalamo yoyenera mfumu imene iye ali. Tsono mitengo yomangira nyumba ya Mulungu uyenera kukhala wabwino. Mpingo woona opangidwa ndi Mulungu osati ndi manja a munthu, opangidwa kuchokera ku miyala yamoyo—Akristu woona—zotsutsana ndi miyala yakufa, kapena njerwa. Yesu amanga ndi miyala yabwino yokha.

Ngati ife takwatirana ndi iye mu pangano ndi lumbira. Kuyisa zikonda zina zonse, kubadwanso kachiwiri, kukhala ndi mitima yofewa, kukonda ziphunzitso zake, kufunitsa kusintha zinthu zofunika kusintha m’moyo wathu. Ndikutembenuza nkhope yathu kwaiye munthawi yazovuta kapena zophinja, kufunsa iye ndi abalendi alongo athu kuti atithandize, ndiye kuti tili mwala wokongola wa moyo wa nyumba yoti Yesu akhalemo. Ungakhale ndipo idzakhala mkwatibwi waulemelero wa Yesu. Uwu ndiye uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu.

jesuslifetogether.com
chiCheŵa Languages icon
 Share icon